["Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa,kapena wosaimirira m'njira ya ochimwa,kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.","Komatu m'chilamulo cha Yehova muli chikondwerero chake;ndipo m'chilamulo chake amalingirira usana ndi usiku.","Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi;wakupatsa chipatso chake pa nyengo yake,tsamba lake lomwe losafota;ndipo zonse azichita apindula nazo.","Oipa satero ai;koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.","Chifukwa chake oipa sadzaimirira pa mlanduwo,kapena ochimwa mu msonkhano wa olungama.","Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama;koma mayendedwe a oipa adzatayika."]