["M'mene Israele anatuluka ku Ejipito,nyumba ya Yakobo kwa anthu a chinenedwe chachilendo;","Yuda anakhala malo ake oyera, Israele ufumu wake.","Nyanjayo inaona, nithawa;Yordani anabwerera m'mbuyo.","Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo,timapiri ngati anaankhosa.","Unathawanji nawe, nyanja iwe?Unabwereranji m'mbuyo, Yordani iwe?","Munatumphatumphiranji ngati nkhosa zamphongo, mapiri inu?Ngati anaankhosa, zitunda inu?","Unjenjemere, dziko lapansi iwe, pamaso pa Ambuye,pamaso pa Mulungu wa Yakobo;","amene anasanduliza thanthwe likhale thawale lamadzi,nsangalabwi ikhale kasupe wamadzi."]