["Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni,tinakhala ngati anthu akulota.","Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka,ndi lilime lathu linafuula mokondwera;pamenepo anati mwa amitundu,Yehova anawachitira iwo zazikulu.","Yehova anatichitira ife zazikulu;potero tikhala okondwera.","Bwezani ukapolo wathu, Yehova,ngati mitsinje ya kumwera.","Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kufuula mokondwera.","Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa;adzabweranso ndithu ndi kufuula mokondwera,alikunyamula mitolo yake."]