["Mudzandiiwala chiiwalire, Yehova, kufikira liti?Mudzandibisira ine nkhope yanu kufikira liti?","Ndidzachita uphungu m'moyo mwanga kufikira liti,pokhala ndi chisoni m'mtima mwanga tsiku lonse?Adzandiukira ine mdani wanga kufikira liti?","Penyani, ndiyankheni, Yehova Mulungu wanga.Penyetsani maso anga, kuti ndingagone tulo ta imfa;","kuti anganene mdani wanga, Ndamlaka;ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.","Koma ine ndakhulupirira pa chifundo chanu;mtima wanga udzakondwera nacho chipulumutso chanu.","Ndidzaimbira Yehova,pakuti anandichitira zokoma."]