["Aleluya.Lemekezani Mulungu m'malo ake oyera;mlemekezeni m'thambo la mphamvu yake.","Mlemekezeni chifukwa cha ntchito zake zolimba;mlemekezeni monga mwa ukulu wake waunjinji.","Mlemekezeni ndi kulira kwa lipenga;mlemekezeni ndi chisakasa ndi zeze.","Mlemekezeni ndi lingaka ndi kuthira mang'ombe:Mlemekezeni ndi zoimbira za zingwe ndi chitoliro.","Mlemekezeni ndi nsanje zomveka:Mlemekezeni ndi nsanje zoliritsa.","Zonse zakupuma zilemekeze Yehova.Aleluya."]